2 Pakuti adzakuonjezera masiku ambiri,Ndi zaka za moyo ndi mtendere.
3 Cifundo ndi coonadi zisakusiye;Uzimange pakhosi pako;Uzilembe pamtima pako;
4 Motero udzapezakisomo ndi nzeru yabwino,Pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse,Osacirikizika pa luntha lako;
6 Umlemekeze m'njira zako zonse,Ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.
7 Usadziyese wekha wanzeru;Opa Yehova, nupatuke pazoipa;
8 Mitsempha yako idzalandirapo moyo,Ndi mafupa ako uwisi.