26 Pakuti Yehova adzalimbitsa mtima wako,Nadzasunga phazi lako lingakodwe.
27 Oyenera kulandira zabwino usawamane;Pokhoza dzanja lako kuwacitira zabwino.
28 Usanene kwa mnzako, Ukabwerenso,Ndipo mawa ndidzakupatsa;Pokhala uli nako kanthu.
29 Usapangire mnzako ciwembu;Popeza akhala nawe pafupi osatekeseka.
30 Usakangane ndi munthu cabe,Ngati sanakucitira coipa,
31 Usacitire nsanje munthu waciwawa;Usasankhe njira yace iri yonse.
32 Pakuti wamphulupulu anyansa Yehova;Koma cinsinsi cace ciri ndi oongoka.