29 Usapangire mnzako ciwembu;Popeza akhala nawe pafupi osatekeseka.
30 Usakangane ndi munthu cabe,Ngati sanakucitira coipa,
31 Usacitire nsanje munthu waciwawa;Usasankhe njira yace iri yonse.
32 Pakuti wamphulupulu anyansa Yehova;Koma cinsinsi cace ciri ndi oongoka.
33 Mulungu atemberera za m'nyumba ya woipa;Koma adalitsa mokhalamo olungama.
34 Anyozadi akunyoza,Koma apatsa akufatsa cisomo.
35 Anzeru adzalandira ulemu colowa cao;Koma opusa adzakweza manyazi.