21 Cifukwa ca zinthu zitatu dziko linthunthumira;Ngakhale cifukwa ca zinai silingathe kupirira nazo:
22 Cifukwa ca kapolo pamene ali mfumu;Ndi citsiru citakhuta zakudya;
23 Cifukwa ca mkazi wodedwa wokwatidwa;Ndi mdzakazi amene adzalandira colowa ca mbuyace.
24 Ziripo zinai ziri zazing'ono padziko;Koma zipambana kukhala zanzeru:
25 Nyerere ndi mtundu wosalimba,Koma zitengeratu zakudya zao m'malimwe.
26 Mbira ndi mtundu wopanda mphamvu,Koma ziika nyumba zao m'matanthwe.
27 Dzombe liribe mfumu,Koma lituruka lonse mabwalo mabwalo.