25 Nyerere ndi mtundu wosalimba,Koma zitengeratu zakudya zao m'malimwe.
26 Mbira ndi mtundu wopanda mphamvu,Koma ziika nyumba zao m'matanthwe.
27 Dzombe liribe mfumu,Koma lituruka lonse mabwalo mabwalo.
28 Buluzi ungamgwire m'manja,Koma ali m'nyumba za mafumu.
29 Pali zinthu zitatu ziyenda cinya cinya;Ngakhale zinai ziyenda mwaufulu:
30 Mkango umene uposa zirombo kulimba,Supambukira cinthu ciri conse;
31 Kavalo wolimba m'cuuno, ndi tonde,Ndi mfumu yokhala ndi ankhondo ace.