12 Mkaziyo amcitira zabwino, si zoipa,Masiku onse a moyo wace.
13 Afuna ubweya ndi thonje,Nacita mofunitsa ndi manja ace.
14 Akunga zombo za malonda;Nakatenga zakudya zace kutari.
15 Aukanso kusanace,Napatsa banja lace zakudya, nagawira adzakazi ace nchito.
16 Asinkhasinkha za munda, naugula;Naoka mipesa ndi zipatso za manja ace.
17 Amanga m'cuuno mwace ndi mphamvu,Nalimbitsa mikono yace,
18 Azindikira kuti malonda ace ampindulira;Nyali yace sizima usiku.