11 Ndakuphunzitsa m'njira ya nzeru,Ndakuyendetsa m'mayendedwe olungama.
12 Mapazi ako sadzaombana ulikuyenda;Ukathamanga, sudzapunthwa.
13 Gwira mwambo, osauleka;Uusunge; pakuti ndiwo moyo wako.
14 Usalowe m'mayendedwe ocimwa,Usayende m'njira ya oipa.
15 Pewapo, osapitamo;Patukapo, nupitirire.
16 Pakuti akapanda kucita zoipa, samagona;Ndipo akapanda kukhumudwitsa wina, tulo tao tiwacokera.
17 Pakuti amadya cakudya ca ucimo,Namwa vinyo wa cifwamba.