18 Koma mayendedwe a olungama akunga kuunika kwa mbanda kuca,Kunkabe kuwala kufikira usana woti mbe.
19 Njira ya oipa ikunga mdima;Sadziwa cimene ciwapunthwitsa,
20 Mwananga, tamvera mau anga;Cherera makutu ku zonena zanga.
21 Asacoke ku maso ako;Uwasunge m'kati mwa mtima wako.
22 Pakuti ali moyo kwa omwe awapeza,Nalamitsa thupi lao lonse.
23 Cinjiriza mtima wako koposa zonse uzisunga;Pakuti magwero a moyo aturukamo.
24 Tasiya m'kamwa mokhota,Uike patari milomo yopotoka.