6 Sasinkhasinkha bwino za njira ya moyo;Mayendedwe ace adzandira dzandi dzandi osadziwa iye.
7 Ndipo tsopano ana, mundimvere,Musapatuke ku mau a m'kamwa mwanga.
8 Siyanitsa njira yako kutari kwa iyeyo,Osayandikira ku khomo la nyumba yace;
9 Kuti ungapereke ulemu wako kwa ena,Ndi zaka zako kwa ankhanza;
10 Kuti mphamvu yako isakhutitse alendo,Ndi kuti usagwire nchito m'nyumba ya wacilendo;
11 Ungalire pa cimariziro cako,Pothera nyama yako ndi thupi lako;
12 Ndi kuti, Bwanji ndinada mwambo,Mtima wanga ndi kunyoza cidzudzulo;