17 Akundikonda ndiwakonda;Akundifunafuna adzandipeza.
18 Katundu ndi ulemu ziri ndi ine,Cuma cosatha ndi cilungamo.
19 Cipatso canga ciposa golidi, ngakhale golidi woyengeka;Phindu langa liposa siliva wosankhika.
20 Ndimayenda m'njira ya cilungamo,Pakati pa mayendedwe a ciweruzo,
21 Kuti ndionetse cuma akundikonda, cikhale colowa cao,Ndi kudzaza mosungira mwao.
22 Mulungu anali nane poyamba njira yace,Asanalenge zace zakale.
23 Anandiimika cikhalire ciyambire,Dziko lisanalengedwe.