20 Ndimayenda m'njira ya cilungamo,Pakati pa mayendedwe a ciweruzo,
21 Kuti ndionetse cuma akundikonda, cikhale colowa cao,Ndi kudzaza mosungira mwao.
22 Mulungu anali nane poyamba njira yace,Asanalenge zace zakale.
23 Anandiimika cikhalire ciyambire,Dziko lisanalengedwe.
24 Pamene panalibe zozama ndinabadwa ine,Pamene panalibe akasupe odzala madzi.
25 Mapiri asanakhazikike,Zitunda zisanapangidwe, ndinabadwa;
26 Asanalenge dziko, ndi thengo,Ngakhale ciyambi ca pfumbi la dziko.