22 Mulungu anali nane poyamba njira yace,Asanalenge zace zakale.
23 Anandiimika cikhalire ciyambire,Dziko lisanalengedwe.
24 Pamene panalibe zozama ndinabadwa ine,Pamene panalibe akasupe odzala madzi.
25 Mapiri asanakhazikike,Zitunda zisanapangidwe, ndinabadwa;
26 Asanalenge dziko, ndi thengo,Ngakhale ciyambi ca pfumbi la dziko.
27 Pamene anakhazika mlengalenga ndinali pompo;Pamene analemba pazozama kwete kwete;
28 Polimbitsa Iye thambo la kumwamba,Pokula akasupe a zozama.