25 Mapiri asanakhazikike,Zitunda zisanapangidwe, ndinabadwa;
26 Asanalenge dziko, ndi thengo,Ngakhale ciyambi ca pfumbi la dziko.
27 Pamene anakhazika mlengalenga ndinali pompo;Pamene analemba pazozama kwete kwete;
28 Polimbitsa Iye thambo la kumwamba,Pokula akasupe a zozama.
29 Poikira nyanja malire ace,Kuti madzi asapitirire pa lamulo lace;Polemba maziko a dziko,
30 Ndinali pa mbali pace ngati mmisiri;Ndinamsekeretsa tsiku ndi tsiku,Ndi kukondwera pamaso pace nthawi zonse;
31 Ndi kukondwera ndi dziko lace lokhalamo anthu,Ndi kusekerera ndi ana a anthu.