3 Pambali pa cipata polowera m'mudzi,Polowa anthu pa makomo ipfuula:
4 Ndinu ndikuitanani, amuna,Mau anga ndilankhula kwa ana a anthu.
5 Acibwana inu, cenjerani,Opusa inu, khalani ndi mtima wozindikira;
6 Imvani, pakuti ndikanena zoposa,Ndi zolungama potsegula pakamwa panga,
7 Pakuti m'kamwa mwanga mudzalankhula ntheradi,Zoipa zinyansa milomo yanga.
8 Mau onse a m'kamwa mwanga alungama;Mwa iwo mulibe zokhota ndi zopotoka.
9 Onsewo amveka ndi iye amene azindikira;Alungama kwa akupeza nzeru.