32 Ndipo tsopano, ananga, mundimvere ine,Ngodala akusunga njira zanga.
33 Imvani mwambo, mukhale anzeru osaukana.
34 Ngwodala amene andimvera, nadikira pa zitseko zanga tsiku ndi tsiku,Ndi kulinda pa mphuthu za makoma anga;
35 Pakuti wondipeza ine apeza moyo;Yehova adzamkomera mnma.
36 Koma wondicimwira apweteka moyo wace;Onse akundida ine akonda imfa.