7 Woweruza munthu wonyoza adzicititsa yekha manyazi;Yemwe adzudzula wocimwa angodetsa mbiri yace yace.
8 Usadzudzule wonyoza kuti angakude;Dzudzula wanzeru adzakukonda.
9 Ukacenjeza wanzeru adzakulitsa nzeru yace;Ukaphunzitsa wolungama adzaonjezera kuphunzira,
10 Ciyambi ca nzeru ndico kuopa Yehova;Kudziwa Woyerayo ndiko luntha;
11 Pakuti mwa ine masiku ako adzacuruka,Zaka za moyo wako zidzaonjezedwa.
12 Ukakhala wanzeru, si yako yako nzeruyo?Ndipo ukanyoza udzasauka wekha.
13 Utsiru umalongolola,Ngwa cibwana osadziwa kanthu.