48 Cifukwa iye anayang'anira umphawi wa mdzakazi wace;Pakuti taonani, kuyambira tsopano, anthu a mibadwo yonse adzandichula ine wodala.
49 Cifukwa iye Wamphamvuyo anandicitira ine zazikuru;4 Ndipo dzina lace liri loyera.
50 5 Ndipo cifundo cace cifikira anthu a mibadwo mibadwoPa iwo amene amuopa iye.
51 Iye anacita zamphamvu ndi mkono wace;6 Iye anabalalitsa odzitama ndi mlingaliro wa mtima wao,
52 iye anatsitsa mafumu pa mipando yao yacifumu,Ndipo anakweza aumphawi,
53 7 Anawakhutitsa anjala ndi zinthu zabwino,Ndipo eni cuma anawacotsa opanda kanthu.
54 Anathangatira Israyeli mnyamata wace,Kuti akakumbukile cifundo,