Luka 14 BL92

Yesu aciritsa munthu wodwala mbulu

1 Ndipo panali pamene iye analowa m'nyumba ya mmodzi wa akuru a Afarisi tsiku la Sabat a, kukadya, iwo analikumzonda iye.

2 Ndipo onani, panali pamaso pace munthu wambulu.

3 Ndipo Yesu anayankha nati kwa acilamulo ndi Afarisi, nanena, Kodi nkuloledwa tsiku la Sabata kuciritsa, kapena iai?

4 Koma iwo anakhala cete. Ndipo anamtenga namciritsa, namuuza apite.

5 Ndipo anati kwa iwo, Ndani wa inu buru wace kapena ng'ombe yace itagwa m'citsime, ndipo sadzaiturutsa pomwepo tsiku la Sabata kodi?

6 Ndipo iwo sanathe kumbwezera mau pa zinthu izi.

Fanizo La mipando ya ulemu

7 Ndipo iye ananena fanizo kwa oitanidwa, popenya kuti amadzisankhira mipando yaulemu, nanena kwa iwo,

8 Pamene pali ponse waitanidwa iwe ndi munthu ku cakudya ca ukwati, usaseama pa mpando waulemu; kuti kapena wina waulemu wakuposa iwe akaitanidwe ndi iye,

9 ndipo pakufika iye amene adaitana iwe ndi uyu, adzati kwa iwe, Mpatse uyu malo; ndipo pomwepo udzayamba manyazi kukhala pa mpando wa kuthungo.

10 Koma pamene pali ponse waitanidwa iwe, pita nukhale pansi pa malo a kuthungo; kotero kuti pamene akadza iye anakuitana iwe, akanena ndi iwe, Bwenzi langa, sendera, kwera kuno; pomwepo udzakhala ndi ulemerero pamaso pa onse akuseama pacakudya pamodzi ndi iwe.

11 Cifukwa munthu ali yense wakudzikuza adzacepetsedwa; ndipo wakudzicepetsa adzakulitsidwa.

12 Ndipo ananenanso kwa iye amene adamuitana, Pamene ukonza cakudya ca pausana kapena ca madzulo, usaitane abwenzi ako, kapena abale ako, kapena a pfuko lako, kapena anansi ako eni cuma; kuti kapena iwonso angabwereze kuitana iwe, ndipo udzakhala nayo mphotho.

13 Koma pamene ukonza phwando uitane aumphawi, opunduka, otsimphina, akhungu;

14 ndipo udzakhala wodala; cifukwa iwo alibe cakubwezera iwe mphotho; pakuti idzabwezedwa mphotho pa kuuka kwa oiungama.

Fanizo la phwando lalikuru

15 Ndipo pamene wina wa iwo akuseama pacakudya pamodzi ndi iye anamva izi, anati kwa iye, Wodala iye amene adzadya mkate mu Ufumu wa Mulungu.

16 Koma anati kwa iye, Munthu wina anakonza phwando lalikuru; naitana anthu ambiri;

17 ndipo anatumiza kapolo wace pa nthawi ya phwando kukanena kwa oitanidwawo, idzani, cifukwa zonse zakonzeka tsopano.

18 Ndipo onse ndi mtima umodzi anayamba kuwiringula. Woyamba anati kwa iye, Ine ndagula munda, ndipo ndiyenera ndituruke kukauona; ndikupempha undilole ine ndisafika.

19 Ndipo anati wina, Ine ndagula ng'ombe za magori asanu, ndipo ndinka kukaziyesa; ndikupempha undilole ine ndisafika.

20 Ndipo anati wina, Ine ndakwatira mkazi, ndipo cifukwa cace sindingathe kudza.

21 Ndipo kapoloyo pakubwera anauza mbuye wace zinthu izi. Pamenepo mwini nyumba anakwiya, nati kwa kapolo wace, Turuka msanga, pita kumakwalala ndi ku njira za mudzi, nubwere nao muno aumphawi ndi opunduka ndi akhungu ndi otsimphina.

22 Ndipo kapoloyo anati, Ambuye, cimene munacilamulira cacitika, ndipo malo atsalapo.

23 Ndipo mbuye ananena kwa kapoloyo, Turuka, nupite kumiseu ndi njira za kuminda, nuwaumirize anthu alowe, kuti nyumba yanga idzale.

24 Pakuti ndinena kwa inu, kuti kulibe mmodzi wa amuna oitanidwa aja adzalawa phwando langa.

Womtsata Ambuye adzayesedwa

25 Ndipo mipingo yambiri ya anthu inamuka naye; ndipo iye anapotoloka, nati kwa iwo.

26 Munthu akadza kwa Ine, wosada atate wace ndi amace, ndi mkazi wace, ndi ana, ndi abale, ndi alongo ace, inde ndi moyo wace womwe wa iye mwini, sakhoza kukhala wophunzira wanga.

27 Ndipo amene ali yense sasenza mtanda wace wa mwini yekha, ndi kudza pambuyo panga, sakhoza kukhala wophunzira wanga,

28 Pakuti ndani wa inu amene akafuna kumanga nsanja yaitali, sathanga wakhala pansi, nawerengera mtengo wace, aone ngati ali nazo zakuimariza?

29 Kuti kungacitike, pamene atakhazika pansi miyala ya ku maziko ace, osakhoza kuimariza, anthu onse akuyang'ana adzayamba kumseka iye,

30 ndi kunena kuti, Munthu uyu anayamba kumanga, koma sanathe kumariza.

Fanizo la mfumu vanzeru

31 Kapena mfumu yanji pakupita kukomana ndi nkhondo ya mfumu inzace, sathanga wakhala pansi, nafunsana ndi akuru ngati akhoza ndi asilikari ace zikwi khumi kulimbana naye wina uja alikudza kukomana naye ndi asilikari zikwi makumi awiri?

32 Koma ngati sakhoza, atumiza akazembe, pokhala winayo ali kutalitali, nafunsa za mtendere.

33 Cifukwa cace tsono, yense wa inu amene sakaniza zonse ali nazo, sakhoza kukhala wophunzira wanga.

34 Kotero mcere uli wokoma; koma ngati mcere utasukuluka adzaukoleretsa ndi ciani?

35 Suyenera kuuthira pamunda kapena padzala, autaya kunja. Amene ali nao makutu akumva amve.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24