50 5 Ndipo cifundo cace cifikira anthu a mibadwo mibadwoPa iwo amene amuopa iye.
51 Iye anacita zamphamvu ndi mkono wace;6 Iye anabalalitsa odzitama ndi mlingaliro wa mtima wao,
52 iye anatsitsa mafumu pa mipando yao yacifumu,Ndipo anakweza aumphawi,
53 7 Anawakhutitsa anjala ndi zinthu zabwino,Ndipo eni cuma anawacotsa opanda kanthu.
54 Anathangatira Israyeli mnyamata wace,Kuti akakumbukile cifundo,
55 8 (Monga analankhula kwa makolo athu)Kwa Abrahamu ndi kwa mbeu yace ku nthawi yonse.
56 Ndipo Mariya anakhala ndi iye ngati miyezi itatu, nabweranso kunyumba kwace.