10 Ndipo analikuphunzitsa m'sungagoge mwina, tsiku la Sabata.
11 Ndipo mkazi anali nao mzimu wakumdwalitsa zaka khumi ndi zisanu ndi zitatu; nakhala wopeteka, ndimo analibe mphamvu konse yakuweramuka.
12 Ndipo Yesu m'mene anamuona, anamuitana, nanena naye, Mkaziwe, wamasulidwa kudwala kwako.
13 Ndipo anaika manja ace pa iye; ndipo pomwepo anaongoledwa, nalemekeza Mulungu.
14 Ndipo mkuru wa sunagoge anabvutika mtima, cifukwa Yesu anaciritsa tsiku la Sabata, nayankha, nanena kwa khamulo, Alipo masiku asanu ndi limodzi, m'menemo anthu ayenera kugwira nchito, cifukwa cace idzani kudzaciritsldwa momwemo, koma tsiku la Sabata ai.
15 Koma Ambuye anamyankha iye, nati, Onyenga inu, kodi munthu ali yense wa inu samaimasula ng'ombe yace, kapena buru wace kucodyeramo, tsiku la Sabata, kupita nayo kukaimwetsa madzi?
16 Ndipo mkazi uyu, ndiye mwana wa Abrahamu, amene Satana anammanga, onani, zaka khumi ndi zisanu ndi zitatu, nanga si kuyenera kodi, kuti amasulidwe nsinga yace imeneyi tsiku la Sabata?