17 Kuti kumwamba ndi dziko lapansi zicoke nkwapafupi, koma kuti kalembo kakang'ono ka cilamulo kagwe nkwapatali.
18 Yense wakusudzula mkazi wace, nakwatira wina, acita cigololo; ndipo iye amene akwatira wosudzulidwayo, acita cigololo,
19 Ndipo panali munthu mwini cuma amabvala cibakuwa ndi nsaru yabafuta, nasekera, nadyerera masiku onse;
20 ndipo wopemphapempha wina, dzina lace Lazaro, adaikidwa pakhomo pace wodzala ndi zironda,
21 ndipo anafuna kukhuta ndi zakugwa pa gome la mwini cumayo; komatu agarunso anadza nanyambita zirondazace.
22 Ndipo kunali kuti wopemphayo adafa, ndi kuti anatengedwa iye ndi angelo kunka ku cifuwa ca Abrahamu; ndipo mwini cumayo adafanso, naikidwa m'manda.
23 Ndipo m'Hade anakweza maso ace, pokhala nao mazunzo, naona Abrahamu patali, ndi Lazaro m'cifuwa mwace.