12 Ndipo m'mene analowa iye m'mudzi wina, anakomana naye amuna khumi akhate, amene anaima kutali;
13 ndipo iwo anakweza mau, nanena, Yesu, Mbuye, muticitire cifundo.
14 Ndipo pakuwaona anati kwa iwo, Pitani, kadzionetseni nokha kwa ansembe. Ndipo kunali, m'kumuka kwao, anakonzedwa.
15 Ndipo mmodzi wa iwo, pakuona kuti anaciritsidwa, anabwerera m'mbuyo, nalemekeza Mulungu ndi mau akuru;
16 ndipo anagwa nkhope yace pansi ku mapazi ace, namyamika iye; ndipo anali Msamariya ameneyo.
17 Ndipo Yesu anayankha nati, Kodi sanakonzedwa khumi? koma ali kuti asanu ndi anai aja?
18 Akubwera kulemekeza Mulungu sanapezeka mmodzi kodi, koma mlendo uyu?