1 Ndipo analowa, napyola pa Yeriko. Ndipo taonani, mwamuna wochedwa dzina lace Zakeyu;
2 ndipo Iye anali mkulu wa amisonkho, nali wacuma.
3 Ndipo anafuna kuona Yesu ndiye uti, ndipo sana the, cifukwa ca khamulo, pakuti anali wamfupi msinkhu.
4 Ndipo anathamanga, natsogola, nakwera mumkuyu kukamuona iye; pakuti anati apite njira yomweyi.