38 Ndipo iye sakhala Mulungu wa akufa, koma wa amoyo: pakuti anthu onse akhala ndi moyo kwa iye.
39 Ndipo alembi ena anayankha nati, Mphunzitsi, mwanena bwino.
40 Pakuti sanalimbanso mtima kumfunsa iye kanthu kena.
41 Koma iye anati kwa iwo, Amanena bwanji kuti Kristuyo ndiye mwana wa Davine?
42 Pakuti Davine yekha anena m'buku la Masalmo,Ambuye ananena kwa Ambuye wanga,Ukhale pa dzanja langa lamanja,
43 Kufikira Ine ndikaika adani akopansi pa mapazi ako.
44 Cotero Davine anamchula iye Ambuye, ndipo nanga ali mwana wace bwanji?