63 Ndipo amuna amene analikusunga Yesu anamnyoza iye, nampanda.
64 Ndipo anamkulunga iye m'maso, namfunsa, nati, Talota; anakupanda Iwe ndani?
65 Ndipo zambiri zina anamnenera iye, namcitira mwano.
66 Ndipo 13 pamene kunaca, bungwe la akuru a anthu linasonkhana, ndiwo ansembe akuru ndi alembi; ndipo anapita naye ku bwalo lao, nanena, 14 Ngati uli Kristu, utiuze.
67 Ndipo anati kwa iwo, Ndikakuuzani, simudzabvomereza;
68 ndipo ndikakufunsani kanthu, simudzayankha.
69 Koma 15 kuyambira tsopano Mwana wa munthu adzakhala pa dzanja lamanja la mphamvu ya Mulungu.