17 Ndipo anapereka kwa iye buku la Yesaya mneneri. Ndipo m'mene iye adafunyulula bukulo, anapeza pomwe panalembedwa,
18 Mzimu wa Ambuye uli paine,Cifukwa cace iye anandidzozaIne ndiuze anthu osauka Uthenga Wabwino:Anandituma Ine kulalikira am'nsinga mamasulidwe,Ndi akhungu kuti apenyenso,Kuturutsa ndi ufuru ophwanyika,
19 Kulalikira caka cosankhika ca Ambuye.
20 Ndipo m'mene iye anapinda bukulo, nalipereka kwa mnyamata, anakhala pansi; ndipo maso ao a anthu onse m'sunagogemo anamyang'anitsa iye.
21 Ndipo anayamba kunena kwa iwo, kuti, Lero lembo ili lakwanitsidwa m'makutu anu.
22 Ndipo onse anamcitira iye umboni nazizwa ndi mau a cisomo akuturuka m'kamwa mwace; nanena, Kodi uyu si mwana wa Yosefe?
23 Ndipo anati kwa iwo, Kwenikweni mudzati kwa Ine nkhani iyi, Sing'anga iwe, tadziciritsa wekha: zonse zija tazimva zinacitidwa ku Kapernao, muzicitenso zomwezo kwanu kuno.