53 Ndipo anamseka iye pwepwete podziwa kuti anafa.
54 Ndipo iye anamgwira dzanja lace, naitana, nati, Buthu, tauka.
55 Ndipo mzimu wace unabwera, ndipo anauka pomwepo; ndipo iye anawauza kuti ampatse kanthu ka kudya.
56 Ndipo atate wace ndi amace anadabwa; ndipo analamulira iwo asauze munthu ali yense cimene cinacitika.