1 Ndipo kunali, pakutsiriza iye kulankhula ndi Sauli, mtima wa Jonatani unalumikizika ndi mtima wa Davide, ndipo Jonatani anamkonda iye monga moyo wa iye yekha.
2 Ndipo Sauli anamtenga tsiku lomwelo, osamlolanso apite kwao kwa atate wace.
3 Pamenepo Jonatani ndi Davide anapangana pangano, pakuti adamkonda iye ngati moyo wa iye yekha.
4 Ndipo Jonatani anabvula maraya ace anali nao, napatsa Davide, ndi zobvala zace, ngakhale lupanga lace, ndi uta wace, ndi lamba lace.