1 Samueli 16 BL92

Samueli adzoza Davide akhale mfumu

1 Ndipo Yehova ananena ndi Samueli, Iwe ukuti ulire cifukwa ca Sauli nthawi yotani, popeza Ine ndinamkana kuti asakhale mfumu ya Israyeli? Dzaza nyanga yako ndi mafuta, numuke, ndidzakutumiza kwa Jese wa ku Betelehemu; pakuti ndinadzionera mfumu pakati pa ana ace.

2 Ndipo Samueli anati, Ndikamuka bwanji? Sauli akacimva, adzandipha. Ndipo Yehova anati, Umuke nayo ng'ombe yaikazi, nunene kuti, Ndadza kudzaphera nsembe kwa Yehova.

3 Ndipo uitane Jese abwere kunsembeko, ndipo Ine ndidzakusonyeza cimene uyenera kucita; ndipo udzandidzozera iye amene ndidzakuchulira dzina lace.

4 Ndipo Samueli anacita cimene Yehova ananena, nadza ku Betelehemu. Ndipo akuru a mudziwo anadza kukomana naye monthunthumira, nati, Mubwera ndi mtendere kodi?

5 Nati iye, Ndi mtendere umene; ndadza kudzaphera nsembe kwa Yehova; mudzipatule ndi kufika ndi ine kunsembeko. Ndipo iye anapatula Jese ndi ana ace, nawaitanira kunsembeko.

6 Ndipo kunali, pakufika iwo, iye anayang'ana pa Eliyabu, nati, Zoonadi, wodzozedwa wa Yehova ali pamaso pace.

7 Koma Yehova ananena ndi Samueli, Vsayang'ane nkhope yace, kapena kutalika kwa msinkhu wace, popeza Ine ndinamkana iye; pakuti Yehova saona monga aona munthu; pakuti munthu ayang'ana cooneka ndi maso, koma Yehova ayang'ana mumtima.

8 Pamenepo Jese anaitana Abinadabu nampititsa pa Samueli. Ndipo iye adati, Koma uyunso Yehova sadamsankha.

9 Pamenepo Jese anapititsapo Sama. Ndipo anati, Koma uyunso Yehova sanamsankha.

10 Ndipo Jese anapititsapo ana ace amuna asanu ndi awiri. Koma Samueli anati kwa Jese, Yehova sanawasankha awa.

11 Ndipo Samueli anati kwa Jese, Ana anu ndi omwewa kodi? Nati iye, Watsala wina, mng'ono wa onse, ndipo taonani, iye alikuweta nkhosa. Ndipo Samueli anati kwa Jese, Tumiza munthu akamtenge; pakuti ife sitidzakhala pansi kufikira iye atadza kuno.

12 Ndipo anatumiza munthu, nabwera naye. Tsono iye anali wofiirira, ndi wa nkhope yokongola, ndi maonekedwe okoma. Ndipo Yehova anati, Nyamuka umdzoze, pakuti ndi ameneyu.

13 Pamenepo Samueli anatenga nyanga ya mafuta, namdzoza pakati pa abale ace; ndipo mzimu wa Yehova unalimbika pa Davide kuyambira tsiku lomweli. Ndipo Samueli ananyamuka, Danks ku Rama.

Davide atumikira Sauli

14 Koma mzimu wa Yehova unamcokera Sauli, ndi mzimu woipa wocokera kwa Yehova unambvuta iye.

15 Ndipo anyamata a Sauli ananena naye, Onani tsopano, mzimu woipa wocokera kwa Mulungu ulikubvuta inu.

16 Tsono inu mbuye wathu muuze anyamata anu, amene ali pamaso panu, kuti afune munthu wanthetemya wodziwa kuyimba zeze; ndipo kudzakhala, pamene mzimu woipa wocokera kwa Mulungu uli pa inu, iyeyo adzayimba ndi dzanja lace, ndipo mudzakhala wolama.

17 Ndipo Sauli anati kwa anyamata ace, Mundifunire tsono munthu wakudziwa kuyimba bwino, nimubwere naye kwa ine.

18 Ndipo mnyamata wace wina anayankha, nati, Taonani, ine ndaona mwana wa Jese wa ku Betelehemu, ndiye wanthetemya wodziwa kuyimbira, ndipo ali wa mtima wolimba ndi woyenera nkhondo, ndiponso ali wocenjera manenedwe ace; ndiye munthu wokongola, ndipo Yehova ali naye.

19 Cifukwa cace Sauli anatumiza mithenga kwa Jese, nati, Vnditumizire Davide, mwana wako, amene ali kunkhosa.

20 Ndipo Jese anatenga buru namsenza mkate, ndi thumba la vinyo, ndi: mwana wa mbuzi, nazitumiza kwa Sauli ndi Davide mwana wace.

21 Ndipo Davide anafika kwa Sauli, naima pamaso pace; ndipo iye anamkonda kwambiri, namsandutsa wonyamula zida zace.

22 Ndipo Sauli anatumiza kwa Jese, nati, Ulole kuti Davide aime pamaso panga; pakuti ndamkomera mtima.

23 Ndipo kunali kuti pamene mzimu woipawo wocokera kwa Mulungu unali pa Sauli, Davide anatenga zeze, naliza ndi dzanja lace; comweco Sauli anatsitsimuka, nakhala bwino, ndi mzimu woipa unamcokeraiye.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24 25 26 27 28 29 30 31