1 Samueli 5 BL92

Likasa la Mulungu ku nyumba ya Dagoni

1 Ndipo Afilisti anatenga likasa la Mulungu, nacoka nalo ku Ebenezeri, napita ku Asidodi.

2 Ndipo Afilistiwo anatenga likasa la Mulungu, nafika nalo ku nyumba ya Dagoni, naliika pafupi ndi Dagoni.

3 Ndipo pakuuka a ku Asidodi mamawa, taonani Dagoni adagwa pansi, nagona cafufumimba patsogolo pa likasa la Yehova. Ndipo iwo anatenga Dagoni namuimikanso m'malo mwace.

4 Ndipo m'mawa mwace polawirira, taonani, Dagoni adagwa pansi, nagona cafufumimba patsogolo pa likasa la Yehova; ndipo mutu wace ndi zikhato zonse ziwiri za manja ace zinagona zoduka paciundo; Dagoni anatsala thupi lokha.

5 Cifukwa cace angakhale ansembe, angakhale ena akulowa m'nyumba ya Dagoni, palibe woponda pa ciundo ca Dagoni ku Asidodi, kufikira lero lino.

Masauko a Afilisti cifukwa ca likasa

6 Koma Yehova anabvuta iwo a ku Asidodi ndi dzanja lace, nawaononga, nawazunza ndi mafundo, m'Asidodi ndi m'miraga yace.

7 Ndipo pamene anthu a ku Asidodi anaona kuti ncomweco, anati iwowa, Likasa la Mulungu wa Israyeli lisakhalitse ndi ife; popeza dzanja lace litiwawira ife, ndi Dagoni mulungu wathu.

8 Cifukwa cace anatumiza mithenga, nasonkhanitsa mafumu onse a Afilisti, nati, Ticite nalo ciani likasa la Mulungu wa Israyeli? Ndipo anati, Anyamule likasa la Mulungu kunka nalo ku Gati, Ndipo ananyamula likasalo la Mulungu wa Israyeli, napita nalo kumeneko.

9 Ndipo kunali atafika nalo, dzanja la Yehova linatsutsa mudziwo ndi kusautsa kwakukuru; ndipo anazunza anthu a mudziwo, akuru ndi ang'ono; ndi mafundo anawabuka.

10 Cifukwa cace anatumiza likasa la Mulungu ku Ekroni. Ndipo kunali pofika likasalo ku Ekroni, a ku Ekroni anapfuula nati, Anadzatitulira likasa la Mulungu wa Israyeli, kutipha ife ndi ana athu.

11 Cifukwa cace anatumiza, nasonkhanitsa mafumu onse a Afilisti, ndipo iwowa anati, Cotsani likasa la Mulungu wa Israyeli, lipitenso kumalo kwace, kuti lingationonge ife, ndi anthu athu; pakuti kunali kusautsa koopsa m'mudzi monse; dzanja la Mulungu linabvutadi pamenepo.

12 Ndipo amene anapanda kufa anagwidwa ndi mafundowo; ndi kulira kwa mudziwo kunakwera kumwamba.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16 17 18 19 20 21 22 23 24 25 26 27 28 29 30 31