19 Ndipo anakantha Nobi ndiwo mudzi wa ansembe ndi lupanga lakuthwa, anthu amuna ndi akazi, ana ndi makanda, ng'ombe ndi aburu, ndi nkhosa, ndi lupanga lakuthwa.
20 Ndipo mmodzi wa ana a Ahimeleki, mwana wa Ahitubu, dzina lace ndiye Abyatara, anapulumuka, nathawira kwa Davide.
21 Ndipo Abyatara anadziwitsa Davide kuti Sauli anapha ansembe a Yehova.
22 Ndipo Davide anati kwa Abyatara, Tsiku lija Doegi wa ku Edomu anali kumeneko, ndinadziwiratu kuti adzauzadi Sauli; ine ndinafetsa anthu onse a nyumba ya atate wako.
23 Ukhale ndi ine, usaopa; popeza iye wakufuna moyo wanga afuna moyo wako; koma ndi ine udzakhala mosungika.