40 Ndipo anyamata a Davide pakufika kwa Abigayeli ku Karimeli, analankhula naye, nati, Davide anatitumiza kwa inu, kukutengani, mukhale mkazi wace.
41 Ndipo iye ananyamuka, nawerama nkhope yace pansi, nati, Onani, mdzakazi wanu ali kapolo wakusambitsa mapazi a anyamata a mbuye wanga.
42 Ndipo Abigayeli anafulumira nanyamuka, nakwera pa bum, pamodzi ndi anamwali ace asanu akumtsata; natsatira mithenga ya Davide, nakhala mkazi wace.
43 Davide anatenganso Ahinoamu wa ku Yezreeli, ndipo onse awiri anakhala akazi ace.
44 Pakuti Sauli anapatsa Mikala, mwana wace, mkazi wa Davide, kwa Paliti mwana wa Loisi, wa ku Galimu.