1 Pamene Ataliya mace wa Ahaziya anaona kuti mwana wace wafa, ananyamuka, naononga mbeu yonse yacifumu.
2 Koma Yoseba mwana wa mfumu Yoramu, mlongo wace wa Ahaziya, anatenga Yoasi mwana wa Ahaziya, namuba pakati pa ana a mfumu akuti aphedwe, iye ndi mlezi, nawaika m'cipinda cogonamo; nambisira Ataliya, ndipo sanaphedwa.
3 Nakhala naye wobisika m'nyumba ya Yehova zaka zisanu ndi cimodzi; ndipo Ataliya anakhala mfumu ya dziko.
4 Koma caka cacisanu ndi ciwiri Yehoyada anaitanitsa atsogoleri a mazana a opha anthu, ndi a otumikira, nabwera nao kwa iye ku nyumba ya Yehova, napangana nao, nawalumbiritsa m'nyumba ya Yehova, nawaonetsa mwana wa mfumu.