13 Ndipo Yoasi anagona ndi makolo ace, ndi Yerobiamu anakhala pa mpando wacifumu wace; namuika Yoasi m'Samariya pamodzi ndi mafumu a Israyeli.
14 Ndipo Elisa anadwala nthenda ija adafa nayo, namtsikira Yoasi mfumu ya Israyeli, namlirira, nati, Atate wanga, atate wanga, gareta wa Israyeli ndi apakavalo ace!
15 Nanena naye Elisa, Tenga uta ndi mibvi; nadzitengera uta ndi mibvi.
16 Nati kwa mfumu ya Israyeli, Pingiridzani. Napingiridza. Ndipo Elisa anasanjika manja ace pa manja a mfumu.
17 Nati, Tsegulani zenera la kum'mawa. Nalitsegula. Nati Elisa, Ponyani. Naponya. Nati iye, Mubvi wa cipulumutso wa Yehova ndiwo mubvi wa kukupulumutsani kwa Aaramu; popeza mudzakantha Aaramu m'Afeki mpaka mudzawatha.
18 Nati iye, Tengani mibvi; naitenga, Nati kwa mfumu ya Israyeli, Kwapula pansi; nakwapula katatu, naleka.
19 Nakwiya naye munthu wa Mulungu, nati, Mukadakwapula kasanu, kapena kasanu ndi kamodzi; mukadatero, mukadadzakantha Aaramu mpaka kuwatha; koma tsopano mudzawakantha Aaramu katatu kokha.