1 Caka caciwiri ca Yoasi mwana wa Yoahazi mfumu ya Israyeli, Amaziya mwana wa Yoasi mfumu ya Yuda analowa ufumu wace.
2 Ndiye wa zaka makumi awiri ndi zisanu polowa ufumu; nakhala mfumu zaka makumi awiri mphambu zisanu ndi zinai m'Yerusalemu; dzina la mace ndiye Yoadana wa ku Yerusalemu.
3 Ndipo anacita zoongoka pamaso pa Yehova, koma wosanga Davide kholo lace; nacita monga mwa zonse anazicita Yoasi atate wace.
4 Koma misanje sanaicotsa; anthu anapherabe nsembe, nafukiza pamisanje.
5 Ndipo kunali, utakhazikika ufumu m'dzanja lace, anakantha anyamata ace amene adakantha mfumu atate wace;
6 koma ana a ambandawo sanawapha, monga mwalembedwa m'buku la cilamulo ca Mose, m'mene adalamulira Yehova, ndi kuti, Atate asaphedwere ana, kapena ana kuphedwera atate; koma yense afere kulak wa kwa iye yekha.