7 Kudatero, popeza ana a Israyeli adacimwira Yehova Mulungu wao, amene anawakweza kuwaturutsa m'dziko la Aigupto pansi pa dzanja la Farao mfumu ya Aigupto, ndipo anaopa milungu yina,
8 nayenda m'miyambo ya amitundu amene Yehova adawaingitsa pamaso pa ana a Israyeli, ndi m'miyambo ya mafumu a Israyeli imene iwo anawalangiza.
9 Ndipo ana a Israyeli anacita m'tseri zinthu zosayenera pa Yehova Mulungu wao, nadzimangira misanje m'midzi mwao monse ku nsanja ya olonda ndi ku mudzi walinga komwe.
10 Nadziimikira zoimiritsa ndi zifanizo pa citunda ciri conse cacitali, ndi patsinde pa mtengo uli wonse wogudira;
11 nafukizapo zonunkhira pa misanje youse, monga umo amacitira amitundu amene Yehova adawacotsa pamaso pao, nacita zoipa kuutsa mkwiyo wa Yehova;
12 natumikira mafano amene Yehova anawanena nao, Musacita ici.
13 Ndipo Yehova anacitira umboni Israyeli ndi Yuda mwa dzanja la mneneri ali yense, ndi mlauli ali yense, ndi kuti, Bwererani kuleka nchito zanu zoipa, nimusunge malamulo anga ndi malemba anga, monga mwa cilamulo conse ndinacilamulira makolo anu, ndi kucitumizira inu mwa dzanja la atumiki anga aneneri.