4 ndiponso cifukwa ca mwazi wosacimwa adaukhetsa; popeza anadzaza Yerusalemu ndi mwazi wosacimwa; ndipo Yehova sanafuna kukhululukira.
5 Macitidwe ena tsono a Yoyakimu, ndi zonse anazicita, sizilembedwa kodi m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda?
6 Nagona Yoyakimu ndi makolo ace, ndipo Yoyakini mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.
7 Koma mfumu ya Aigupto sinabwerezanso kuturuka m'dziko lace, pakuti mfumu ya Babulo idalanda kuyambira ku mtsinje wa Aigupto kufikira ku mtsinje Firate, ndilo lonse anali nalo mfumu ya Aigupto.
8 Yoyakini anali wa zaka khumi mphambu zisanu ndi zitatu polowa iye ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu miyezi itatu; ndi dzina la mace ndiye Nehusita mwana wa Elinatani wa ku Yerusalemu.
9 Nacita iye coipa pamaso pa Yehova, monga umo monse adacita atate wace.
10 Nthawi ija anyamata a Nebukadinezara mfumu ya Babulo anakwerera Yerusalemu, naumangira mudziwo misasa.