1 Ndipo kunali caka cacisanu ndi cinai ca ufumu wace, mwezi wakhumi, tsiku lakhumi la mwezi, Nebukadinezara mfumu ya Babulo, iye ndi khamu lace lonse anadzera Yerusalemu, naumangira misasa, naumangira timalinga mouzinga.
2 Ndipo mudziwo unazingidwa ndi timalinga mpaka caka cakhumi ndi cimodzi ca mfumu Zedekiya.
3 Tsiku lacisanu ndi cinai la mwezi wacinai njala idakula m'mudzimo, panalibe cakudya kwa anthu a m'dzikomo.
4 Pamenepo linga la mudziwo linagamulidwa, nathawira ankhondo onse usiku, njira ya ku cipata ca pakati pa makoma awiri, iri ku munda wa mfumu; Akasidi tsono anali pamudzi pouzinga; nimuka mfumu pa njira ya kucidikha.