26 Pamenepo ananyamuka anthu onse ang'ono ndi akuru, ndi akazembe a makamu, nadza ku Aigupto; pakuti anaopa Akasidi.
27 Ndipo kunali caka ca makumi atatu mphambu zisanu ndi ziwiri ca kumtenga ndende Yoyakini mfumu ya Yuda, mwezi wakhumi ndi ziwiri, tsiku la makumi awiri mphambu asanu ndi awiri la mwezi, Evili Merodaki mfumu ya Babulo anamuweramutsa mutu wace wa Yoyakini mfumu ya Yuda aturuke m'kaidi, caka colowa iye ufumu wace;
28 nakamba naye zokoma, namkweza mpando wace waulemu upose mipando ya mafumu anali pamodzi naye m'Babulo.
29 Nasintha zobvala zace za m'kaidi, namadya iye mkate pamaso pace masiku onse a moyo wace.
30 Ndi kunena za cakudya cace, panali cakudya cosalekeza copatsidwa kwa iye ndi mfumu, tsiku Uri lonse gawo lace, masiku onse a moyo wace.