5 Koma nkhondo ya Akastdi inalondola mfumu, niipeza m'zidikha za Yeriko; koma nkhondo yace yonse inambalalikira.
6 Ndipo anaigwira mfumu, nakwera nayo kwa mfumu ya Babulo ku Ribila, naweruza mlandu wace.
7 Napha ana a Zedekiya pamaso pace, namkolowola Zedekiya maso ace, nammanga ndi maunyolo amkuwa, namuka nave ku Babulo.
8 Ndipo mwezi wacisanu, tsiku lacisanu ndi ciwiri la mweziwo, ndico caka cakhumi mphambu cisanu ndi cinai ca mfumu Nebukadinezara mfumu ya Babulo, Nebuzaradani mkuru wa olindirira, ndiye mnyamata wa mfumu ya Babulo, anadza ku Yerusalemu,
9 natentha nyumba ya Yehova, ndi nyumba ya mfumu, ndi nyumba zonse za m'Yerusalemu; ndi nyumba zonse zazikuru anazitentha ndi moto.
10 Ndi khamu lonse la Akasidi linali ndi mkuru wa olindirira linagumula linga la Yerusalemu louzinga.
11 Ndi anthu otsalira m'mudzi, ndi opanduka akuthawira kwa mfumu ya Babulo, ndi aunyinji otsalira, Nebuzaradani mkuru wa olindirira anamuka nao andende.