2 Ndipo Elisa anati kwa iye, Ndikucitire ciani? undiuze m'nyumba mwako muli ciani? Nati, Mdzakazi wanu alibe kanthu m'nyumba, koma mtsuko wa mafuta.
3 Pamenepo anati, Kabwereke zotengera kwina kwa anansi ako onse, zotengera zopanda kanthu, zisakhale pang'ono.
4 Nulowe, uudzitsekere wekha ndi ana ako amuna ndi kutsanulira m'zotengera zonsezi, nuike padera zodzalazo.
5 Pamenepo anamcokera, nadzitsekera yekha ndi ana ace amuna; iwo namtengera zotengerazo, iye namatsanulira.
6 Ndipo kunali, zitadzala zotengera, anati kwa mwana wace, Nditengere cotengera cina, Nanena naye, Palibe cotengera cina. Ndipo mafuta analeka.
7 Pamenepo anadza, namfotokozera munthu wa Mulungu. Nati iye, Kagulitse mafuta, ukabwezere mangawa ako, ndi zotsalapo zikusunge iwe ndi ana ako.
8 Ndipo linafika tsiku lakuti Elisa anapitirira kumka ku Sunemu, kumeneko kunali mkazi womveka; ameneyo anamuumiriza adye mkate. Potero pomapitirako iyeyu, adafowapa, mbukirako kukadya mkate.