33 Nati iye, Mgwetsereni pansi. Namgwetsera pansi, nuwazikako mwazi wace pakhoma ndi pa akavalo, nampondereza iye pansi.
34 Ndipo atalowa, anadya namwa, nati, Kampenyeni tsono mkazi wotembereredwa uyu, nimumuike; popeza ndiye mwana wa mfumu.
35 Namuka iwo kuti amuike; koma sanapezako kanthu kena koma bade, ndi mapazi, ndi zikhato za manja.
36 Nabwerera iwo, namfotokozera. Nati iye, Ndiwo mau a Yehova ananena wo mwa mtumiki wace Eliya wa ku Tisibe, ndi koti, Pa munda wa Yezreeli agaru adzadya mnofu wa Yezebeli;
37 ndi thupi la Yezebeli lidzakhala ngati ndowe pamunda m'dera la Yezreeli, kuti sadzati, Ndi Yezebeli uyu.