4 Mkazi wodekha ndiye korona wa mwamuna wace;Koma wocititsa manyazi akunga cobvunditsa mafupa a mwamunayo.
5 Maganizo a olungama ndi ciweruzo;Koma uphungu wa oipa unyenga.
6 Mau a oipa abisalira mwazi;Koma m'kamwa mwa olungama muwalanditsa.
7 Oipa amagwa kuli zi;Koma banja la olungama limaimabe.
8 Munthu amatamandidwa monga mwa nzeru yace;Koma wokhota mtima adzanyozedwa.
9 Wonyozedwa, amene ali ndi kapolo,Aposa wodzikuza, amene asowa zakudya.
10 Wolungama asamalira moyo wa coweta cace;Koma cifundo ca oipa ndi nkhanza.