3 Maso a Yehova ali ponseponse,Nayang'anira oipa ndi abwino.
4 Kuciza lilime ndiko mtengo wa moyo;Koma likakhota liswa moyo.
5 Citsiru cipeputsa mwambo wa atate wace;Koma wosamalira cidzudzulo amacenjera.
6 M'nyumba ya wolungama muli katundu wambiri;Koma m'phindu la woipa muli bvuto,
7 Milomo ya anzeru iwanditsa nzeru,Koma mtima wa opusa suli wolungama.
8 Nsembe ya oipa inyansa Yehova;Koma pemphero la oongoka mtima limkondweretsa.
9 Njira ya oipa inyansa Yehova;Koma akonda wolondola cilungamo.