10 Ukainga wonyoza, makangano adzaturuka;Makani ndi manyazi adzalekeka.
11 Wokonda kuyera mtima,Mfumu idzakhala bwenzi lace cifukwa ca cisomo ca milomo yace.
12 Maso a Yehova acinjiriza wodziwa;Koma agwetsa mau a munthu wa ziwembu.
13 Waulesi ati, Pali mkango panjapo,Ndidzaphedwa pamakwalalapo.
14 M'kamwa mwa mkazi waciwerewere muli dzenje lakuya;Yemwe Yehova amkwiyira adzagwamo.
15 Utsiru umangidwa mumtima mwa mwana;Koma ntyole yomlangira idzauingitsira kutari.
16 Wotsendereza waumphawi kuti acurukitse cuma cace,Ndi wopatsa wolemera kanthu, angosauka.