7 Wolemera alamulira osauka;Ndipo wokongola ndiye kapolo wa womkongoletsa.
8 Wofesa zosalungama adzakolola tsoka;Ndipo ntyole ya mkwiyo wace idzalephera.
9 Mwini diso lamataya adzadala;Pakuti apatsa osauka zakudya zace.
10 Ukainga wonyoza, makangano adzaturuka;Makani ndi manyazi adzalekeka.
11 Wokonda kuyera mtima,Mfumu idzakhala bwenzi lace cifukwa ca cisomo ca milomo yace.
12 Maso a Yehova acinjiriza wodziwa;Koma agwetsa mau a munthu wa ziwembu.
13 Waulesi ati, Pali mkango panjapo,Ndidzaphedwa pamakwalalapo.