12 Ukanena, Taonani, sitinadziwa cimeneci;Kodi woyesa mitima sacizindikira ici?Ndi wosunga moyo wako kodi sacidziwa?Ndipo kodi sabwezera munthu yense monga mwa macitidwe ace?
13 Mwananga, idya uci pakuti ngwabwino,Ndi cisa cace citsekemera m'kamwamwako;
14 Potero udzadziwa kuti nzeru iri yotero m'moyo wako;Ngati waipeza padzakhala mphotho,Ndipo ciyembekezo cako sicidzalephereka.
15 Usabisalire, woipa iwe, pomanga wolungama;Usapasule popuma iyepo.
16 Pakuti wolungama amagwa kasanu ndi kawiri, nanyamukanso;Koma oipa akhumudwa pomfikira tsoka.
17 Usakondwere pakugwa mdani wako;Mtima wako usasekere pokhumudwa iye;
18 Kuti Yehova angaone kukondwa kwako, ndi kukuyesa koipa,Ndi kuleka kumkwiyira.