6 Pakuti udzaponya nkhondo yako ndi upo,Ndi kupulumuka pocuruka aphungu,
7 Nzeru itarikira citsiru;Satsegula pakamwa kubwalo.
8 Wolingalira zakucita zoipaAnthu adzamcha waciwembu.
9 Maganizo opusa ndiwo cimo;Wonyoza anyansa anthu.
10 Ukalefuka tsiku la tsokaMphamvu yako icepa.
11 Omwe atengedwa kuti akafe, uwapulumutse;Omwe ati aphedwe, usaleke kuwalanditsa.
12 Ukanena, Taonani, sitinadziwa cimeneci;Kodi woyesa mitima sacizindikira ici?Ndi wosunga moyo wako kodi sacidziwa?Ndipo kodi sabwezera munthu yense monga mwa macitidwe ace?