1 Mau a Aguri mwana wa Yake; uthenga. Munthuyo anati, Ndadzitopetsa, Mulungu;Ndadzitopetsa, Mulungu, ndathedwa;
2 Pakuti ndipambana anthu onse kupulukira,Ndiribe luntha la munthu.
3 Sindinaphunzira nzeruNgakhale kudziwa Woyerayo.
4 Ndani anakwera kumwamba natsikanso?Ndani wakundika nafumbata mphepo?Ndani wamanga madzi m'maraya ace?Ndani wakhazikitsa matsiriziro onse a dziko?Dzina lace ndani? dzina la mwanace ndani? kapena udziwa.
5 Mau onse a Mulungu ali oyengeka;Ndiye cikopa ca iwo amene amkhulupirira.
6 Usaoniezere kanthu pa mau ace,Angakudzudzule, nungatsutsidwe kuti ulikunama.
7 Zinthu ziwiri ndakupemphani,Musandimane izo ndisanamwalire: