4 Ndani anakwera kumwamba natsikanso?Ndani wakundika nafumbata mphepo?Ndani wamanga madzi m'maraya ace?Ndani wakhazikitsa matsiriziro onse a dziko?Dzina lace ndani? dzina la mwanace ndani? kapena udziwa.
5 Mau onse a Mulungu ali oyengeka;Ndiye cikopa ca iwo amene amkhulupirira.
6 Usaoniezere kanthu pa mau ace,Angakudzudzule, nungatsutsidwe kuti ulikunama.
7 Zinthu ziwiri ndakupemphani,Musandimane izo ndisanamwalire:
8 Mundicotsere kutari zacabe ndi mabodza;Musandipatse umphawi, ngakhale cuma,Mundidyetse zakudya zondiyenera;
9 Ndingakhute ndi kukukanani, ndi kuti, Yehova ndani?Kapena ndingasauke ndi kuba,Ndi kuchula dzina la Mulungu wanga pacabe.
10 Usanamizire kapolo kwa mbuyace,Kuti angakutemberere nawe ndi kutsutsidwa.